Nkhaniyi ikuti mwana wa mkazi wa mkuluyo adakwatiwa ndi m’nyamata wina ndipo awiriwo amakhala ku chikamwini kutanthauza kuti amakhala kwao kwa mkaziyo. Koma chodabwitsa nchakuti m’nyamatayo wakhala pa banjapo miyezi yochepa yokha kotero kuti apongozi ake a amuna ake amamuchitiranso Nsanje. Ndipo pomaliza pake anamuthamangitsa pakhomopo ponena kuti adalakwitsa mwana wake kukwatiwa ndi kapunthabuye yemwe sangathandize mwana waoyo. Kamba ka izi m’nyamatayo anamulozera njira ya kwao ngakhale kuti m’nyamatayo amakhala bwino lomwe ndi mkazi wake popanda chovuta. Koma mikoko yogona pamudzipo itafufuza yapeza kuti mkuluyo wathamangitsa mkamwiniyo kamba koti amasokoneza mapulani ake. Ndipo malume wa mtsikanayo anakadandaula nkhaniyi ku bwalo la anyakwawa omwe ataitanitsa mkuluyo anamulamula kulipira chindapusa komanso kuti achoke pamudzipo pakutha pa sabata azipita kwao kamba koti zomwe wachitazo ndi zolaula mudzi. Pakadalipano mkuluyo sakutuluka m’nyumba kamba ka manyazi chifukwa choti nkhaniyi yawanda m’deralo.
M'busa wina amuthamangitsa ku Mulanje
Mbusa wa mpingo wina ku Thuchila m’boma la Mulanje amusamutsira ku Blantyre akhristu olusa atafuna kumukuntha kamba ka khalidwe lake lopasula komanso lodzetsa udani pakati pa akhristu. Nkhaniyi ikuti mbusayo yemwe akuti ndi wokonda kwambiri ndalama komanso wakhala akulalatira akhristuwo ponena kuti sakupereka moolowa manja. Komiti yapa mpingowo potopa ndi zimenezi inapereka lipoti ku likulu la mpingowu ku Blantyre. Ndipo aku likuluwo anatumiza nthumwi zomwe zitakafufuza za madandaulowo zapeza kuti zomwe akhristuwo amadandaula ndi zoona ndipo pakadalipano m’busayo amusamutsira ku Blantyre. Akhristu pa mpingowo apempha ku likulu la mpingowo kuti pamene akuganizira zowatumizira mbusa awatumizire munthu yemwe adaitanidwa kugwira ntchito ya Chauta.