Nkhani-yi ikuti mai-yu yemwe ali ndi zaka pafupifupi makumi asanu anakhala pa banja zaka zoposa makumi atatu moti ali ndi zidzukulu. Mai-yu akuti anakwatila ndi mwamuna yemwe amakonda ulimi. Ndipo nthawi zambiri mwamuna-yo amatumiza mkazi-yo kumudzi kuti akalime. Mwamuna-yo akuti amapatsa mkazi-yo ndalama zambiri kuti mkazi-yo asamasowe kanthu akapita ku mudzi-ko. Koma mmalo mochita zolima mkazi-yo akuti anapalana ubwenzi ndi mkulu wina. Anthu ena anatsina khutu mwamuna wa mkazi-yi za ubwenzi wa awiri-wo.
Amukwangwanula zofunda
Mnyamata wina pa sukulu yaukachenjede yotchuka kwambiri ku Blantyre anagwidwa njakata mkulu yemwe anamutengela foni ncholinga choti amugulitsile atamukwangwanula zofunda. Makolo a mnyamata-yo akuti ndi opeza bwino kwambiri moti ndalama sivuto. Makolo-wo akuti amapatsa mnyamata-yo zonse zomwe amafuna koma zimathela mowa ndi zibwenzi. Mnyamata-yo akuti akatumizilidwa zinthu monga foni kapena laptop amagulitsa pa mtengo ozizila kwambiri bola apeze ya kabanga. Munthu wina akuti anapatsa mnyamata-yo foni ya mtengo wapatali kuti amugulitsile ku sukulu kwao. Mnyamata-yo akuti anayamba kutsatsa lamya-yo pa mtengo wa 30 thousand Kwacha. Koma kenaka anatsitsa mpaka munthu wina anagula foni-yo pa mtengo wa 10 thousand Kwacha. Mmalo mokapereka ndalama kwa mwini foni mnyamata-yo akuti anamwera mowa ndalama-yo. Ndipo patapita masiku ochepa mwini foni uja anafika ku malo komwe mnyamata-yo amagona kukatenga ndalama yake. Uko mnyamata-yo anapanga chibwibwi. Mwini lamya-yo ataona kuti mnyamata-yo wamupusitsa akuti anakwiya kwambiri ndipo anangotenga zofunda zonse za mnyamata-yo. Kwa masiku angapo mnyamata-yo anakhala akubwereka zofunda kwa amzake koma ataona kuti sizimuthandiza mnyamata-yo akuti wapiti kwao pomwe zikukaiktsa kuti abwerelanso ku sukulu kamba koti watenga katundu wake yense.