You are here:CategoriesNkhani Zam'maboma14/07/15

14/07/15

Written by  Newsroom

Awilikiza chisembwere ndi ana osapola nchomba
Mayi wina mdera la mfumu Mabuka m’boma la Mulanje akudabwitsa athu powilikiza kuchita zachisembwere ndi ana osapola pa mchombo.

15
July

Nkhani-yi ikuti mai-yu yemwe ali ndi zaka pafupifupi makumi asanu anakhala pa banja zaka zoposa makumi atatu moti ali ndi zidzukulu. Mai-yu akuti anakwatila ndi mwamuna yemwe amakonda ulimi. Ndipo nthawi zambiri mwamuna-yo amatumiza mkazi-yo kumudzi kuti akalime. Mwamuna-yo akuti amapatsa mkazi-yo ndalama zambiri kuti mkazi-yo asamasowe kanthu akapita ku mudzi-ko. Koma mmalo mochita zolima mkazi-yo akuti anapalana ubwenzi ndi mkulu wina. Anthu ena anatsina khutu mwamuna wa mkazi-yi za ubwenzi wa awiri-wo.

 

 

Amukwangwanula zofunda
Mnyamata wina pa sukulu yaukachenjede yotchuka kwambiri ku Blantyre anagwidwa njakata mkulu yemwe anamutengela foni ncholinga choti amugulitsile atamukwangwanula zofunda. Makolo a mnyamata-yo akuti ndi opeza bwino kwambiri moti ndalama sivuto. Makolo-wo akuti amapatsa mnyamata-yo zonse zomwe amafuna koma zimathela mowa ndi zibwenzi. Mnyamata-yo akuti akatumizilidwa zinthu monga foni kapena laptop amagulitsa pa mtengo ozizila kwambiri bola apeze ya kabanga. Munthu wina akuti anapatsa mnyamata-yo foni ya mtengo wapatali kuti amugulitsile ku sukulu kwao. Mnyamata-yo akuti anayamba kutsatsa lamya-yo pa mtengo wa 30 thousand Kwacha. Koma kenaka anatsitsa mpaka munthu wina anagula foni-yo pa mtengo wa 10 thousand Kwacha. Mmalo mokapereka ndalama kwa mwini foni mnyamata-yo akuti anamwera mowa ndalama-yo. Ndipo patapita masiku ochepa mwini foni uja anafika ku malo komwe mnyamata-yo amagona kukatenga ndalama yake. Uko mnyamata-yo anapanga chibwibwi. Mwini lamya-yo ataona kuti mnyamata-yo wamupusitsa akuti anakwiya kwambiri ndipo anangotenga zofunda zonse za mnyamata-yo. Kwa masiku angapo mnyamata-yo anakhala akubwereka zofunda kwa amzake koma ataona kuti sizimuthandiza mnyamata-yo akuti wapiti kwao pomwe zikukaiktsa kuti abwerelanso ku sukulu kamba koti watenga katundu wake yense.

About us

Malawi Broadcasting Corporation is a public broadcaster mandated and formed by Government under an Act of Parliament in 1964, to enhance the successful implementation of all its social and economic programs...

Social Media

Catch us on these social networks for more information

Facebook Twitter RSS

Get Your Newsletter