Athamangitsidwa paukwati kamba kachiwerewere
Mai wina pamudzi wa Holowani kwa Kadewere mboma la Chiradzulu amuthamangitsa pa ukwati ku Lilongwe chifukwa chokonda chiwelewele mwamuna wake akatalikira pakhomo.
Athamangitsidwa pa ukwati kamba ka umbombo
Mkulu wina kwa Senzani mboma la Ntcheu amuthamangitsa pa ukwati chifukwa cha umbombo. Nkhaniyi ikuti mkuluyo anakwatira pamudzipo zaka ziwiri zapitazi koma mkaziyo anamupeza ndi ana akunjira awiri amuna okhaokha a zaka zosaposera khumi.
Mkazi wachibwenzi afika panyumba kuzasiya zovala
Mkulu wina wakwa Santhe pa msika mboma la Kasungu akuyenda moziya kwambili chifukwa cha manyazi, mkazi wa chibwenzi atadzamusiila zovala kuphatikizapo makabudula amkati pamaso pa mkazi wake.
Achilapa atakwera mumtengo ataledzera
Mkulu wina mdera la mfumu Nkalo mboma la Chiladzulu wanenetsa kuti sadzachitanso matama okwera mu mtengo ataledzera.